Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Ndili M’manja Mwanu

Ndili M’manja Mwanu

Citani daunilodi:

  1. 1. Yehova M’lungu mumaona

    Za mumtima wanga wocimwa

    Pamene n’kutumikilani.

    Ningalankhule mawu oipa

    Kapena kucita zoipa,

    Nipempha, “Nithandizileni.”

    (MWANA WA KOLASI)

    Ndinu Atate wanga

    Ndipo ine ndinetu dongo.

    (KOLASI)

    Munganiumbe kukhala

    Munthu wabwino zedi,

    Yemwe inu mungamukonde.

    Umbeni mwacikondi

    Nikhale bwenzi lanu.

    Atate nipempha!

    Umbeni ine.

    Umbeni ine.

  2. 2. Nikamawelenga mawu anu

    Ndi kucita zomwe mufuna,

    Mumtima nimamvela bwino.

    Nipatseni mtima womvela

    Kuti nizicita zoyenela.

    Zolakwa zisanilefule.

    (MWANA WA KOLASI)

    Ndinu Atate wanga

    Ndipo ine ndinetu dongo

    (KOLASI)

    Munganiumbe kukhala

    Munthu wabwino zedi,

    Yemwe inu mungamukonde.

    Umbeni mwacikondi

    Nikhale bwenzi lanu.

    Atate nipempha!

    Umbeni ine.

    Umbeni ine.

    (KUMALIZA)

    Conde n’thadizeni

    Nikhale womvela.

    Atate nipempha!

    Umbeni ine,

    Umbeni ine.