Privacy Settings

To provide you with the best possible experience, we use cookies and similar technologies. Some cookies are necessary to make our website work and cannot be refused. You can accept or decline the use of additional cookies, which we use only to improve your experience. None of this data will ever be sold or used for marketing. To learn more, read the Global Policy on Use of Cookies and Similar Technologies. You can customize your settings at any time by going to Privacy Settings.

Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

Munthu wa ku Middle East akupemphela.

Mulungu “Wakumva pemphelo,” amakondwela kutimvetsela.—SALIMO 65:2

Pitilizani Kupemphela Kuti Mulungu Akuyanjeni

Pitilizani Kupemphela Kuti Mulungu Akuyanjeni

Mulungu anapatsa ife anthu mphatso yapadela yakuti tizikwanitsa kukambilana naye m’pemphelo, na kumuuza mmene timvelela. Mneneli Davide anapemphela kuti: “Inu Wakumva pemphelo, anthu a mitundu yonse adzabwela kwa inu.” (Salimo 65:2) Koma kodi tingapemphele bwanji kuti Mulungu atimvele na kutidalitsa?

PEMPHELANI MODZICEPETSA KOMANSO MOCOKELA PANSI PAMTIMA

Mapemphelo anu a panokha amakupatsani mwayi wokhuthulila Mulungu za mumtima mwanu, kuti mumuuze zokhudza mmene mumvelela. (Salimo 62:8) Mulungu Wamphamvuzonse amakonda mapemphelo ocokela pansi pamtima.

POKAMBA NA MULUNGU MUZISEŴENZETSA DZINA LAKE LENI-LENI

Ngakhale kuti Mulungu ali na maina audindo ambili, dzina lake leni-leni ni limodzi. Iye akuti, “Ine ndine Yehova. Dzina langa ndi limeneli.” (Yesaya 42:8) Dzina lakuti Yehova limapezeka maulendo opitilila 7,000 m’Malemba Oyela. Popemphela kwa Mulungu, aneneli ambili anali kuseŵenzetsa dzina lake leni-leni. Abulahamu anati: “Conde Yehova, . . . ndiloleni ndilankhulebe [nanu].” (Genesis 18:30) Nafenso tiyenela kuseŵenzetsa dzina la Mulungu lakuti Yehova popemphela.

PEMPHELANI M’CITUNDU CIMENE MUFUNA

Mulungu amamvetsetsa maganizo athu na mmene timvelela, mosasamala kanthu za citundu cimene timakamba. Mawu ake amatitsimikizila kuti: “Mulungu alibe tsankho. Iye amalandila munthu wocokela mu mtundu uliwonse, amene amamuopa ndi kucita cilungamo.”—Machitidwe 10:34, 35.

Koma kuwonjezela pa kupemphela, palinso zina zimene tifunika kucita kuti tidalitsidwe na Mulungu. M’nkhani zokonkhapo, tidzaona zimene tifunika kucita.