Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

CUMA COPEZEKA M’MAU A MULUNGU | YOHANE 7-8

Yesu Analemekeza Atate Wake

Yesu Analemekeza Atate Wake

7:15-18, 28, 29; 8:29

Mu zokamba na zocita zake zonse, Yesu analemekeza Atate wake wakumwamba. Anali kufuna kuti anthu adziŵe kuti uthenga wake unali wocokela kwa Mulungu. Conco, Malemba ndiwo anali maziko a ziphunzitso zake, ndipo kaŵili-kaŵili anali kugwila mau Malemba. Akatamandidwa, Yesu anali kupeleka citamandoco kwa Yehova. Cacikulu kwa iye cinali kukwanilitsa nchito imene Yehova anam’patsa.—Yoh. 17:4.

Tingatengele bwanji citsanzo ca Yesu . . .

  • potsogoza phunzilo la Baibo kapena pophunzitsa pa pulatifomu?

  • pamene anthu ena atitamanda?

  • poganizila mmene tingaseŵenzetsele nthawi yathu?