December 30, 2024–January 5, 2025
MASALIMO 120-126
Nyimbo 144 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)
Aisiraeli amene anabwelela kwawo akukolola mbewu mwacisangalalo cifukwa Yehova wadalitsa khama lawo
1. Anabyala Akulila, koma Anakolola Akusangalala
(Mph. 10)
Aisiraeli anasangalala atamasulidwa ku ukapolo ku Babulo kuti akabwezeletse kulambila koona (Sal. 126:1-3)
Aisiraeli amene anabwelela ku Yudeya analila, mwina cifukwa ca kukula kwa nchito imene anafunika kugwila (Sal. 126:5; w04-CN 6/1 16 ¶10)
Koma iwo analimbikila kugwila nchitoyo ndipo anadalitsidwa (Sal. 126:6; w21.11 24 ¶17; w01-CN 7/15 18-19 ¶13-14; onani cithunzi )
ZOFUNIKA KUZISINKHASINKHA: Pambuyo populumutsidwa pa nkhondo ya Aramagedo, kodi n’zovuta ziti zimene tidzakumana nazo pokonzanso dzikoli? Nanga tidzapeza madalitso otani?
2. Kufufuza Cuma Cauzimu
(Mph. 10)
-
Sal. 124:2-5—Kodi tiyenela kuyembekezela kuti Yehova adzateteza moyo wathu ngati mmene anacitila kwa Aisiraeli? (cl-CN 73 ¶15)
-
Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?
3. Kuŵelenga Baibo
(Mph. 4) Sal. 124:1–126:6 (th phunzilo 5)
4. Kuyambitsa Makambilano
(Mph. 3) ULALIKI WAPOYELA. (lmd phunzilo 3 mfundo 5)
5. Kubwelelako
(Mph. 4) KUNYUMBA NA NYUMBA. Pa makambilano apita, munthuyo anaonetsa kuti sakhulupilila Baibo. (lmd phunzilo 9 mfundo 5)
6. Kupanga Ophunzila
Nyimbo 155
7. Kondwelani na Malonjezo a Mulungu
(Mph. 15.) Kukambilana.
Yehova anakwanilitsa zimene analonjeza kwa anthu amene anagwidwa ukapolo ku Babulo. Anawapulumutsa na kuwacilitsa mwauzimu. (Yes. 33:24) Iye anateteza anthuwo komanso ziweto zawo ku mikango yolusa komanso zilombo zina zimene zinali zitaculuka pa nthawiyo. (Yes. 65:25) Iwo anali kukhala m’nyumba zawo-zawo komanso kudya zipatso za m’minda yawo ya mpesa. (Yes. 65:21) Mulungu anadalitsa nchito yawo, ndipo iwo anakhala na moyo wautali.—Yes. 65:22, 23.
Waterfall: Maridav/stock.adobe.com; mountains: AndreyArmyagov/stock.adobe.com
Tambitsani VIDIYO Yakuti Kondwelani na Malonjezo a Mulungu Okamba za Mtendele—Mbali Yake. Ndiyeno funsani omvela kuti:
-
Kodi maulosi amenewa akukwanilitsika motani masiku ano?
-
Nanga adzakwanilitsika motani pa mlingo waukulu m’dziko latsopano?
-
Kodi ni ulosi uti umene inu mukuuyembekezela mwacidwi?
8. Phunzilo la Baibo la Mpingo
(Mph. 30) bt mutu 20 ¶8-12, bokosi pa tsa. 161