CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU
Cuma Sicimapangitsa Munthu Kukhala Wolungama
Cuma Sicimapangitsa Munthu Kukhala Wolungama
Zofari anakamba kuti Mulungu amalanda cuma ca anthu oipa. Pokamba mawuwa, iye anali kutanthauza kuti Yobu ayenela kuti anacimwa (Yobu 20:5, 10, 15)
Yobu anamuyankha kuti: ‘Nanga n’cifukwa ciyani anthu oipa amalemela?’ (Yobu 21:7-9)
Citsanzo ca Yesu cionetsa kuti ngakhale munthu wolungama akhoza kukhala wopanda cuma (Luka 9:58)
ZOYENELA KUZISINKHASINKHA: Kodi cofunika kwambili kwa munthu wolungama n’ciyani, mosasamala kanthu kuti ni wolemela kapena wosauka?—Luka 12:21; w07 8/1 29 ¶12.