July 1-7
MASALIMO 57-59
Nyimbo 148 na Pemphelo | Mawu Oyamba (Mph. 1)
Mfumu Sauli na amuna amene anali naye pambuyo polephela kugwila Davide
1. Yehova Amasokoneza Olimbana na Anthu Ake
(Mph. 10)
Davide anakakamizika kuthaŵa Mfumu Sauli (1 Sam. 24:3; Sal. 57, tumawu twapamwamba)
Yehova analepheletsa ziwembu za anthu amene anali kulimbana na Davide (1 Sam. 24:7-10, 17-22; Sal. 57:3)
Nthawi zambili ziwembu za anthu olimbana nafe sizikwanilitsa colinga cawo (Sal. 57:6; bt-CN 220-221 ¶14-15)
DZIFUNSENI KUTI, ‘Ningaonetse bwanji kuti nimadalila Yehova pamene nikuzunzidwa?’—Sal. 57:2.
2. Kufufuza Cuma Cauzimu
(Mph. 10)
Sal. 57:7—Kodi kukhala wotsimikiza mtima kumatanthauza ciyani? (w23.07 18-19 ¶16-17)
Pa kuŵelenga Baibo kwa mlungu uno, munapeza mfundo zothandiza ziti zimene mungakonde kutifotokozelako?
3. Kuŵelenga Baibo
(Mph. 4) Sal. 59:1-17 (th phunzilo 12)
4. Khama—Mmene Paulo Anaonetsela Khalidwe Limeneli
(Mph. 7) Kukambilana. Tambitsani VIDIYO, kenako kambilanani lmd phunzilo 7 mfundo 1-2.
5. Khama—Tengelani Citsanzo ca Paulo
(Mph. 8) Makambilano ozikika mu lmd phunzilo 7 mfundo 3-5, komanso mbali yakuti “Onaninso Malemba Awa.”
Nyimbo 65
6. Zofunikila za Mpingo
(Mph. 15)
7. Phunzilo la Baibo la Mpingo
(Mph. 30) bt mutu 12 ¶1-6, bokosi pa tsa. 96