Onani zimene zilipo

Onani nkhani zake

CUMA COPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | 2 ATESALONIKA 1-3

Wosamvela Malamulo Aonekela

Wosamvela Malamulo Aonekela

2:6-12

Kodi Paulo anali kutanthauza ciani pa mavesiwa?

  • ‘Cocititsa’ (vs. 6)—Mwacionekele ni atumwi

  • ‘Kuonekela’ (vs. 6)—Atumwi atamwalila, Akhristu a mpatuko anaonekela poyela n’kuyamba kuphunzitsa zinthu zabodza na kucita zinthu mwacinyengo

  • “Cinsinsi ca kusamvela malamulo” (vs. 7)—“Wosamvela malamulo” sanadziŵike bwino-bwino m’nthawi ya Paulo

  • “Wosamvela malamulo” (vs. 8)—Masiku ano ni atsogoleli onse a machalichi acikhristu

  • “Ambuye Yesu adzamuthetsa [wosamvela malamulo]. . . pa nthawi imene kukhalapo kwa Yesuyo kudzaonekele “ (vs. 8)—Yesu adzaonetsa poyela kuti ni Mfumu akadzapeleka ciweluzo ca Yehova pa dongosolo lino la Satana, komanso kwa “wosamvela malamulo”

Kodi mavesiwa akulimbikitsani bwanji pa nkhani ya kulalikila mwakhama ndiponso mwacangu?