Zokhudza Kusunga Chinsinsi

Pofuna kukuthandizani kuti musamavutike kuchita zinthu pawebusaiti yathu, timagwiritsa ntchito ma cookies ndiponso njira zina zamakono zofanana ndi zimenezi. Ma cookies ena amathandiza kuti webusaiti yathu izigwira bwino ntchito ndipo sizingatheke kuwakana. Mukhoza kuvomereza kapena kukana ma cookies ena owonjezera, omwe cholinga chake ndi kungokuthandizani kuti musamavutike kuchita zinthu zina pawebusaiti. Sitidzagulitsa kapena kugwiritsa ntchito mauthenga amenewa pofuna kutsatsa malonda. Kuti mudziwe zambiri, werengani Ndondomeko ya Padziko Lonse ya Mmene Timagwiritsira Ntchito ma Cookies ndi Njira Zina Zamakono. Mukhoza kusintha ma settings nthawi ina iliyonse popita pa Zokhudza Kusunga Chinsinsi.

Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Nyimbo 140

Moyo wa Mpainiya

Moyo wa Mpainiya

(Mlaliki 11:6)

  1. M’mawa uliwonse, tulo tisanathe,

    Timadzuka n’kupita

    kolalikira uthenga.

    Ndipo Mulungu amatitsogolera

    Timakondwa anthu

    akamamvetsera uthenga.

    (KOLASI)

    Tinasankha,

    kutumikira Yehova.

    Timachita zofuna zake.

    Tipitirizabe kulalikiraku,

    Tikatero timasonyeza

    Chikondi.

  2. Pofika madzulo, timatopa ndithu

    Komabe timapeza

    chimwemwe potumikira

    Madalitso Yehova amatipatsa

    Nthawi zonse

    timamuthokoza potithandiza.

    (KOLASI)

    Tinasankha,

    kutumikira Yehova.

    Timachita zofuna zake.

    Tipitirizabe kulalikiraku,

    Tikatero timasonyeza

    Chikondi.