Zokhudza Kusunga Chinsinsi

Pofuna kukuthandizani kuti musamavutike kuchita zinthu pawebusaiti yathu, timagwiritsa ntchito ma cookies ndiponso njira zina zamakono zofanana ndi zimenezi. Ma cookies ena amathandiza kuti webusaiti yathu izigwira bwino ntchito ndipo sizingatheke kuwakana. Mukhoza kuvomereza kapena kukana ma cookies ena owonjezera, omwe cholinga chake ndi kungokuthandizani kuti musamavutike kuchita zinthu zina pawebusaiti. Sitidzagulitsa kapena kugwiritsa ntchito mauthenga amenewa pofuna kutsatsa malonda. Kuti mudziwe zambiri, werengani Ndondomeko ya Padziko Lonse ya Mmene Timagwiritsira Ntchito ma Cookies ndi Njira Zina Zamakono. Mukhoza kusintha ma settings nthawi ina iliyonse popita pa Zokhudza Kusunga Chinsinsi.

Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

Bambo ndi mwana wake akukonza njinga limodzi

MUTU 7

Zimene Mungachite Pophunzitsa Mwana Wanu

Zimene Mungachite Pophunzitsa Mwana Wanu

“Mawu awa amene ndikukulamula lero azikhala pamtima pako, ndi kuwakhomereza mwa ana ako.”—Deuteronomo 6:6, 7

Yehova amafuna kuti makolo azitsogolera ana awo. (Akolose 3:20) Choncho makolo ali ndi udindo wophunzitsa ana awo kuti azikonda Yehova komanso kuti adzakhale anthu odalirika. (2 Timoteyo 1:5; 3:15) Makolo ayeneranso kudziwa zimene zili mumtima mwa ana awo. Musaiwale kuti ana amatsatira zimene mumachita. Choncho Mawu a Yehova ayenera kukhala mumtima mwanu choyamba kuti muphunzitse bwino ana anu.—Salimo 40:8.

1 ATHANDIZENI KUTI AZIMASUKA NANU

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Aliyense akhale wofulumira kumva, wodekha polankhula.” (Yakobo 1:19) Muzithandiza ana anu kuti azimasuka kulankhula nanu. Ana ayenera kudziwa kuti mukhoza kuwamvetsera nthawi iliyonse imene akufuna kukuuzani zinazake. Mukamakhala mwamtendere m’banja mwanu, ana amamasuka kufotokoza maganizo awo. (Yakobo 3:18) Koma sangamasuke akaona kuti mukhoza kukwiya kapena kuwadzudzula akakuuzani zinazake. Muyenera kuwalezera mtima ndipo muziwatsimikizira kuti mumawakonda.—Mateyu 3:17; 1 Akorinto 8:1.

ZIMENE MUNGACHITE:

  • Muzimvetsera ana anu akafuna kulankhula nanu

  • Muzilankhulana ndi ana anu nthawi zonse osati pakakhala vuto basi

2 MUZIYESETSA KUMVETSA MAGANIZO AWO

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Munthu wosonyeza kuzindikira pa zinthu adzapeza zabwino.” (Miyambo 16:20) Nthawi zina mwana akalankhula musamaganizire zimene wanena koma zimene akutanthauza komanso mmene akumvera mumtima mwake. Achinyamata amakonda kukokomeza zinthu kapena kulankhula zina koma akutanthauza zina. Paja Baibulo limati: “Munthu aliyense woyankhira nkhani asanaimvetsetse n’ngopusa.” (Miyambo 18:13) Choncho musamafulumire kukwiya.—Miyambo 19:11.

Mayi akukalipira mwana wake chifukwa cha zimene mwanayo wangowauza

ZIMENE MUNGACHITE:

  • aya mwana wanu alankhule zotani, yesetsani kuti musamudule mawu kapena kumupsera mtima

  • Muzikumbukira mmene munkamvera muli msinkhu wakewo komanso zimene munkaona kuti n’zofunika

3 MUZICHITA ZINTHU MOGWIRIZANA

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Mwana wanga, tamvera malangizo a bambo ako, ndipo usasiye malamulo a mayi ako.” (Miyambo 1:8) Yehova wapereka udindo wolera ana kwa bambo komanso mayi. Muyenera kuphunzitsa ana anu kuti azikulemekezani ndiponso kukumverani. (Aefeso 6:1-3) Ana amadziwa ngati makolo awo ‘sagwirizana.’ (1 Akorinto 1:10) Ngati simunagwirizane pa nkhani inayake, muziyesetsa kuti ana anu asaone zimenezi chifukwa angasiye kukulemekezani.

Bambo watengera pambali mwana wake kuti amulangize pomwe ana ena ali m’chipinda china

ZIMENE MUNGACHITE:

  • Muyenera kugwirizana zimene muzichita polangiza ana anu

  • Ngati mukusiyana maganizo pa nkhaniyi, yesetsani kumvetsa zimene mnzanuyo akufuna

4 MUZIGWIRIZANA MMENE MUNGAWAPHUNZITSIRE

ZIMENE BAIBULO LIMANENA: “Phunzitsa mwana m’njira yomuyenerera.” (Miyambo 22:6) Sikuti kuphunzitsa bwino ana anu kumangochitika kokha. Koma muyenera kugwirizana zimene muzichita powaphunzitsa ndiponso kuwalangiza. (Salimo 127:4; Miyambo 29:17) Muyenera kuthandiza ana kumvetsa ubwino wa malamulo anu komanso zifukwa zimene mumawalangira. (Miyambo 28:7) Muziwaphunzitsanso kukonda Mawu a Yehova ndiponso kumvetsa mfundo zake. (Salimo 1:2) Zimenezi zingawathandize kukhala ndi chikumbumtima chabwino.—Aheberi 5:14.

ZIMENE MUNGACHITE:

  • Muziyesetsa kuthandiza ana anu kuti adziwe bwino Mulungu n’kumamudalira

  • Muziwathandiza kuzindikira ndiponso kupewa zinthu zoipa zimene zimapezeka pa Intaneti. Muziwaphunzitsanso mmene angapewere ogwirira ana

Makolo akuphunzitsa mwana wawo kuyambira ali wamng’ono mpaka kubatizidwa

“Phunzitsa mwana m’njira yomuyenerera”