Pitani ku nkhani yake # link, for screen reader ##

Pitani ku mitu ya nkhani

CHUMA CHOPEZEKA M’MAWU A MULUNGU | GENESIS 44-45

Yosefe Anakhululukira Azichimwene Ake

Yosefe Anakhululukira Azichimwene Ake

44:1, 2, 33, 34; 45:4, 5

Kukhululuka kumakhala kovuta makamaka ngati munthu watikhumudwitsa mwadala. Kodi n’chiyani chinathandiza Yosefe kukhululukira azichimwene ake atamulakwira?

  • Yosefe sanabwezere azichimwene ake koma anawakhululukira ataona kuti asintha.​—Sal. 86:5; Luka 17:3, 4

  • Iye sanawasungire chakukhosi koma m’malomwake anatsanzira Yehova amene amakhululuka ndi mtima wonse.​—Mika 7:18, 19

Kodi ndingatsanzire bwanji Yehova pa nkhani yokhululuka?