Kwa wotsogolera nyimbo. Nyimbo ndi Salimo la Davide.
65 Inu Mulungu, tidzakutamandani mu Ziyoni,+Tidzakwaniritsa malonjezo athu kwa inu.+
2 Inu Wakumva pemphero, anthu a mitundu yonse adzabwera kwa inu.+
3 Zolakwa zanga zandikulira,+Koma inu mumatikhululukira machimo athu.+
4 Wosangalala ndi munthu amene inu mwamusankha nʼkumubweretsa pafupi ndi inu,Kuti akhale mʼmabwalo anu.+
Tidzakhutira ndi zinthu zabwino zamʼnyumba yanu,+Kachisi wanu woyera.*+
5 Mudzatiyankha pochita zinthu zachilungamo zomwe ndi zochititsa mantha,+Inu Mulungu amene mumatipulumutsa.Anthu amene amakhala kumbali zonse za dziko lapansi amakudalirani+Kuphatikizapo amene amakhala kutali, kutsidya la nyanja.
6 Ndi mphamvu zanu, munakhazikitsa mapiri mʼmalo ake,Inu muli ndi mphamvu zochuluka.+
7 Mumachititsa kuti nyanja imene ikuchita mafunde ikhale bata.+Mumaletsa phokoso la mafunde ake komanso chipwirikiti cha mitundu ya anthu.+
8 Anthu okhala mʼmadera akutali adzachita mantha ndi zizindikiro zanu.+Mudzachititsa kuti anthu amene amakhala kumene dzuwa limatulukira mpaka kumene limalowera afuule mosangalala.
9 Inu mumasamalira dziko lapansi,Mumalichititsa kuti libale zipatso zambiri* komanso kuti likhale lachonde.+
Mtsinje wochokera kwa Mulungu ndi wodzadza ndi madzi.Mumachititsa kuti dziko lapansi lipereke chakudya kwa anthu,+Umu ndi mmene dziko lapansi munalipangira.
10 Mumanyowetsa minda yake komanso kusalaza dothi limene lalimidwa,*Mumaifewetsa ndi mvula yamvumbi. Mumadalitsa zomera zake.+
11 Chaka mumachiveka zinthu zabwino ndipo zimakhala ngati mwachiveka chisoti chachifumu.Munjira zanu mumakhala zinthu zambiri zabwino.*+
12 Mʼmalo odyetserako ziweto amʼchipululu muli msipu wambiri.*+Ndipo zitunda zavekedwa chisangalalo.+
13 Malo odyetserako ziweto adzaza ndi nkhosa,Ndipo mʼzigwa muli tirigu yekhayekha.+
Malo onsewa akufuula komanso kuimba mosangalala.+
^ Kapena kuti, “Malo oyera.”
^ Kapena kuti, “lisefukire ndi zokolola.”
^ Kapena kuti, “kusalaza mizere yake.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “Njira zanu zimakha mafuta.”
^ Mʼchilankhulo choyambirira, “mukukha mafuta.”


KOPERANI
Baibulo la Dziko Latsopano la Malemba Opatulika (Lokonzedwanso mu 2023)
Masalimo
- 1
- 2
- 3
- 4
- 5
- 6
- 7
- 8
- 9
- 10
- 11
- 12
- 13
- 14
- 15
- 16
- 17
- 18
- 19
- 20
- 21
- 22
- 23
- 24
- 25
- 26
- 27
- 28
- 29
- 30
- 31
- 32
- 33
- 34
- 35
- 36
- 37
- 38
- 39
- 40
- 41
- 42
- 43
- 44
- 45
- 46
- 47
- 48
- 49
- 50
- 51
- 52
- 53
- 54
- 55
- 56
- 57
- 58
- 59
- 60
- 61
- 62
- 63
- 64
- 65
- 66
- 67
- 68
- 69
- 70
- 71
- 72
- 73
- 74
- 75
- 76
- 77
- 78
- 79
- 80
- 81
- 82
- 83
- 84
- 85
- 86
- 87
- 88
- 89
- 90
- 91
- 92
- 93
- 94
- 95
- 96
- 97
- 98
- 99
- 100
- 101
- 102
- 103
- 104
- 105
- 106
- 107
- 108
- 109
- 110
- 111
- 112
- 113
- 114
- 115
- 116
- 117
- 118
- 119
- 120
- 121
- 122
- 123
- 124
- 125
- 126
- 127
- 128
- 129
- 130
- 131
- 132
- 133
- 134
- 135
- 136
- 137
- 138
- 139
- 140
- 141
- 142
- 143
- 144
- 145
- 146
- 147
- 148
- 149
- 150