Salimo 56:1-13

Kwa wotsogolera nyimbo pa “Nkhunda Yosanena Kanthu” pakati pa okhala kutali. Salimo la Davide. Mikitamu.* Pa nthawi imene Afilisiti anamugwira ku Gati.+ 56  Ndikomereni mtima inu Mulungu wanga, chifukwa munthu wopanda pake akufuna kundiwakha ndi pakamwa pake.+Akulimbana nane tsiku lonse ndi kundipondereza.+   Tsiku lonse adani anga akufuna kundiwakha ndi pakamwa pawo,+Pakuti anthu ambiri akumenyana nane modzikuza.+   Ine ndidzadalira inu, tsiku lililonse limene ndingachite mantha.+   Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu, ndidzatamanda mawu ake.+Ine ndimadalira Mulungu, sindidzaopa.+Kodi munthu angandichite chiyani?+   Tsiku lonse amasokoneza zolinga zanga.Nthawi zonse amaganiza zondichitira zoipa.+   Amandiukira ndi kundibisalira,+Iwo nthawi zonse amaonetsetsa mmene ndikuyendera,+Pamene akundidikirira kuti awononge moyo wanga.+   Atayeni chifukwa cha zochita zawo zoipa.+Inu Mulungu, gwetsani mitundu ya anthu mu mkwiyo wanu.+   Inu mwalemba za kuthawathawa kwanga.+Sungani misozi yanga m’thumba lanu lachikopa.+Kodi misozi yanga sili m’buku lanu?+   Pa nthawi imeneyo adani anga adzabwerera pa tsiku limene ndidzaitana inu.+Ndikudziwa bwino kuti Mulungu ali kumbali yanga.+ 10  Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Mulungu,+ ndidzatamanda mawu ake.Popeza kuti ndine wogwirizana ndi Yehova, ndidzatamanda mawu ake.+ 11  Ine ndimadalira Mulungu. Sindidzaopa.+Kodi munthu wochokera kufumbi angandichite chiyani?+ 12  Inu Mulungu, ine ndikuyenera kukwaniritsa malonjezo anga kwa inu.+Ndidzapereka kwa inu nsembe zoyamikira.+ 13  Pakuti inu mwalanditsa moyo wanga ku imfa.+Inu mwateteza phazi langa kuti lisapunthwe,+Kuti ndiyendeyende pamaso pa Mulungu m’kuwala kumene kumaunikira anthu amoyo.+

Mawu a M'munsi

Onani mawu a m’munsi pa Sl 16:Kamutu.