Ekisodo 6:1-30

6  Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: “Tsopano uona zimene ndichite kwa Farao.+ Chifukwa cha dzanja lamphamvu, iye awalola kuchoka, ndipo chifukwa cha dzanja lamphamvu awatulutsa m’dziko lake.”+  Mulungu ananenanso kwa Mose kuti: “Ine ndine Yehova.+  Ndinali kuonekera kwa Abulahamu,+ Isaki+ ndi Yakobo+ monga Mulungu Wamphamvuyonse.+ Koma za dzina langa lakuti Yehova,+ ine sindinadzidziwikitse+ kwa iwo.  Ndinakhazikitsa pangano langa ndi iwo kuti ndidzawapatsa dziko la Kanani, dziko limene anali kukhalamo monga alendo.+  Motero ineyo ndamva kubuula kwa ana a Isiraeli,+ amene Aiguputo akuwagwiritsa ntchito yaukapolo, ndipo ndikukumbukira pangano langa.+  “Choncho uwauze ana a Isiraeli kuti, ‘Ine ndine Yehova. Ndithu, ndidzakutulutsani mu Iguputo ndi kukuchotserani goli lawo, ndipo ndidzakulanditsani ku ukapolo wawo.+ Ndidzakuwombolani ndi dzanja langa lotambasula komanso ndi ziweruzo zamphamvu.+  Chotero ndidzakutengani kukhala anthu anga,+ ndi kukusonyezani kuti ndine Mulungu.+ Inuyo mudzadziwadi kuti ine ndine Yehova Mulungu wanu, amene ndidzakutulutsani mu Iguputo, ndi kukuchotserani goli lawo.+  Ine ndidzakulowetsani m’dziko limene ndinalumbirira+ Abulahamu, Isaki ndi Yakobo, nditakweza dzanja langa. Ndidzakupatsani dzikolo kukhala lanu.+ Ine ndine Yehova.’”+  Kenako Mose analankhula mawu amenewa kwa ana a Isiraeli, koma iwo sanamvere Mose chifukwa chokhumudwa ndiponso chifukwa cha ntchito yowawa ya ukapolo.+ 10  Ndiyeno Yehova anauza Mose kuti: 11  “Pita kwa Farao, mfumu ya Iguputo,+ ukamuuze kuti alole ana a Isiraeli kutuluka m’dziko lake.”+ 12  Koma Mose anayankha Yehova kuti: “Komatu ana a Isiraeli sanandimvere,+ nanga Farao akandimvera bwanji?+ Pakuti ndimalankhula movutikira.”*+ 13  Koma Yehova anapitirizabe kuuza Mose ndi Aroni, kuti apereke lamulo kwa ana a Isiraeli ndi kwa Farao, mfumu ya Iguputo, kuti atulutse ana a Isiraeli m’dziko la Iguputo.+ 14  Tsopano awa ndiwo atsogoleri a nyumba ya makolo a Aisiraeli. Ana aamuna a Rubeni, yemwe anali mwana woyamba kubadwa wa Isiraeli,+ anali Hanoki, Palu, Hezironi ndi Karami.+ Amenewa ndiwo mabanja a fuko la Rubeni.+ 15  Ndipo ana aamuna a Simiyoni anali Yemueli, Yamini, Ohadi, Yakini, Zohari ndi Shauli, mwana amene anabereka ndi mkazi wachikanani.+ Amenewa ndiwo mabanja a fuko la Simiyoni.+ 16  Awa ndi mayina a ana aamuna a Levi,+ malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo:+ Gerisoni, Kohati ndi Merari.+ Ndipo Levi anakhala ndi moyo zaka 137. 17  Ana a Gerisoni anali Libini ndi Simeyi,+ malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo.+ 18  Ndipo ana a Kohati anali Amuramu, Izara, Heburoni ndi Uziyeli.+ Kohati anakhala ndi moyo zaka 133. 19  Ndipo ana aamuna a Merari anali Mali ndi Musi.+ Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo.+ 20  Tsopano Amuramu anatenga Yokebedi, mlongo wa bambo ake, kukhala mkazi wake.+ Ndipo Yokebedi anam’berekera Amuramu, Aroni ndi Mose.+ Amuramu anakhala ndi moyo zaka 137. 21  Ndipo ana aamuna a Izara anali Kora,+ Nefegi ndi Zikiri. 22  Ndipo ana aamuna a Uziyeli anali Misayeli, Elizafana ndi Sitiri.+ 23  Aroni anatenga Eliseba, mwana wamkazi wa Aminadabu, mlongo wake wa Naasoni,+ kukhala mkazi wake. Ndipo Eliseba anam’berekera Nadabu, Abihu, Eleazara ndi Itamara.+ 24  Ndipo ana aamuna a Kora anali Asiri, Elikana ndi Abiasafu.+ Amenewa ndiwo anali mabanja a Kora.+ 25  Ndipo Eleazara mwana wa Aroni,+ anatenga mwana wamkazi wa Putieli kukhala mkazi wake. Ndipo iye anam’berekera Pinihasi.+ Amenewa ndiwo atsogoleri a mabanja a m’fuko la Levi, malinga ndi mzere wobadwira wa makolo awo.+ 26  Umenewu ndiwo mzere wa Aroni ndi Mose, amene Yehova anawauza kuti:+ “Tulutsani ana a Isiraeli m’dziko la Iguputo malinga ndi makamu awo.”+ 27  Mose ndi Aroni amenewa ndi amene analankhula kwa Farao mfumu ya Iguputo, kuti atulutse ana a Isiraeli mu Iguputo.+ 28  Choncho pa tsiku limene Yehova analankhula ndi Mose m’dziko la Iguputo,+ 29  Yehova anamuuza kuti: “Ine ndine Yehova.+ Zonse zimene ndikukuuza, ukauze Farao mfumu ya Iguputo.” 30  Pamenepo Mose anauza Yehova kuti: “Komatu ndimalankhula movutikira, ndiye Farao akandimvera bwanji?”+

Mawu a M'munsi

Mawu ake enieni, “Ndine wosadulidwa milomo,” ngati kuti milomo yake inali ndi khungu lolendewera, moti inali yaitali kwambiri ndi yochindikala, yomulepheretsa kulankhula bwinobwino.